23. Ndipo ndidzaphwanya omsautsa pamaso pace;Ndidzapandanso odana naye.
24. Koma cikhulupiriko canga ndi cifundo canga zidzakhala naye;Ndipo nyanga yace idzakwezeka m'dzina langa.
25. Ndipo ndidzaika dzanja lace panyanja,Ndi dzanja lamanja lace pamitsinje.