Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:12-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.

13. Muli nao mkono wanu wolimba;M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

14. Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu;Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.

15. Odala anthu odziwa liu la lipenga;Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

16. Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse;Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.

17. Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao;Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.

18. Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.

19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.

21. Amene dzanja langa lidzakhazikika naye;Inde mkono wanga udzalimbitsa.

22. Mdani sadzamuumira mtima;Ndi mwana wa cisalungamo sadzamzunza.

23. Ndipo ndidzaphwanya omsautsa pamaso pace;Ndidzapandanso odana naye.

24. Koma cikhulupiriko canga ndi cifundo canga zidzakhala naye;Ndipo nyanga yace idzakwezeka m'dzina langa.

25. Ndipo ndidzaika dzanja lace panyanja,Ndi dzanja lamanja lace pamitsinje.

26. Iye adzandichula, ndi kuti, Inu ndinu Atate wanga,Mulungu wanga, ndi thanthwe la cipulumutso canga.

27. Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba,Womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89