Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:11-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu;Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.

12. Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.

13. Muli nao mkono wanu wolimba;M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

14. Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu;Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.

15. Odala anthu odziwa liu la lipenga;Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

16. Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse;Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.

17. Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao;Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.

18. Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.

19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.

21. Amene dzanja langa lidzakhazikika naye;Inde mkono wanga udzalimbitsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89