11. Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu;Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.
12. Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.
13. Muli nao mkono wanu wolimba;M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.
14. Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu;Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.
15. Odala anthu odziwa liu la lipenga;Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.
16. Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse;Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.
17. Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao;Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.