Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzayimbira zacifundo za Yehova nthawi yonse:Pakamwa panga ndidzadziwitsira cikhulupiriko canu ku mibadwo mibadwo.

2. Pakuti ndinati, Cifundo adzacimanga kosaleka;Mudzakhazika cikhulupiriko canu m'Mwamba mweni mweni.

3. Ndinacita cipangano ndi wosankhika wanga,Ndinalumbirira Davide mtumiki wanga:

4. Ndidzakhazika mbeu yako ku nthawi yonse,Ndipo ndidzamanga mpando wacifumu wako ku mibadwo mibadwo.

5. Ndipo kumwamba kudzalemekeza zodabwiza zanu, Yehova;Cikhulupiriko canunso mu msonkhano wa oyera mtima.

6. Pakuti kuli yani kuthambo timlinganize ndi Yehova?Afanana ndi Yehova ndani mwa ana a amphamvu?

7. Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri m'upo wa oyera mtima,Ndiye wocititsa mantha koposa onse akumzinga.

8. Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova?Ndipo cikhulupiriko canu cikuzingani.

9. Inu ndinu wakucita ufumu pa kudzikuza kwa nyanja;Pakuuka mafunde ace muwacititsa bata.

10. Mudathyola Rahabu, monga munthu wophedwa;Munabalalitsa adani anu ndi mkono wa mphamvu yanu.

11. Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu;Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.

12. Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89