Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 86:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Amitundu onse mudawalenga adzadza nadzagwada pamaso panu, Ambuye; Nadzalemekeza dzina lanu.

10. Pakuti Inu ndinu wamkulu, ndi wakucita zodabwiza;Inu ndinu Mulungu, nokhanu.

11. Mundionetse njira yanu, Yehova; ndidzayenda m'coonadi canu:Muumbe mtima wanga ukhale umodzi kuti uliope dzina lanu.

12. Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.

13. Pakuti cifundo canu ca pa ine ncacikuru;Ndipo munalanditsa moyo wanga kunsi kwa manda.

14. Mulungu, odzikuza andiukira,Ndi msonkhano wa anthu oopsa afuna moyo wanga,Ndipo sanaika Inu pamaso pao.

15. Koma Inu, Ambuye, ndinu Mulungu wansoni ndi wacisomo,Wosapsa mtima msanga, ndi wocurukira cifundo ndi coonadi.

16. Mundibwerere ine, ndi kundicitira cifundo;Mpatseni mtumiki wanu mphamvu yanu,Ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17. Mundicitire cizindikilo coti cabwino;Kuti ondida acione, nacite manyazi,Popeza Inu, Yehova, munandithandiza ndi kundisangalatsa,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 86