Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 86:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pakati pa milungu palibe wina wonga Inu, Ambuye;Ndipo palibe nchito zonga zanu.

9. Amitundu onse mudawalenga adzadza nadzagwada pamaso panu, Ambuye; Nadzalemekeza dzina lanu.

10. Pakuti Inu ndinu wamkulu, ndi wakucita zodabwiza;Inu ndinu Mulungu, nokhanu.

11. Mundionetse njira yanu, Yehova; ndidzayenda m'coonadi canu:Muumbe mtima wanga ukhale umodzi kuti uliope dzina lanu.

12. Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 86