Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 86:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mundicitire cifundo, Ambuye;Pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.

4. Kondwetsani moyo wa mtumiki wanu;Pakuti ndikwezera moyo wanga kwa Inu, Ambuye.

5. Pakuti fnu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira,Ndi wa cifundo cocurukira onse akuitana Inu.

6. Cherani khutu pemphero langa, Yehova;Nimumvere mau a kupemba kwanga,

7. Tsiku la msauko wanga ndidzaitana Inu;Popeza mudzandibvomereza.

8. Pakati pa milungu palibe wina wonga Inu, Ambuye;Ndipo palibe nchito zonga zanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 86