1. Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!
2. Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova;Mtima wanga ndi thupi langa zipfuulira kwa Mulungu wamoyo.
3. Mbawanso inapeza nyumba,Ndi namzeze cisa cace coikamo ana ace,Pa maguwa a nsembe anu, Yehova wa makamu,Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,
4. Odala iwo akugonera m'nyumba mwanu;Akulemekezani cilemekezere,
5. Wodala munthu amene mphamvu yace iri mwa Inu;Mumtima mwace muli makwalala a ku Ziyoni,
6. Popyola cigwa ca kulira misozi aciyesa ca akasupe;Inde mvula: ya cizimalupsa icidzaza ndi madalitso.
7. Apita mwamphamvu naonjezapo mphamvu,Aoneka pamaso pa Mulungu m'Ziyoni.