Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 82:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,Ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3. Weruzani osauka ndi amasiye;Weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4. Pulumutsani osauka ndi aumphawi:Alanditseni m'dzanja la oipa,

5. Sadziwa, ndipo sazindikira;Amayendayenda mumdima;Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6. Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,Ndi ana a Wam'mwambamwamba nonsenu.

7. Komatu mudzafa monga anthu,Ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8. Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;Pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 82