Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 82:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,Aweruza pakati pa milungu.

2. Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,Ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3. Weruzani osauka ndi amasiye;Weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4. Pulumutsani osauka ndi aumphawi:Alanditseni m'dzanja la oipa,

5. Sadziwa, ndipo sazindikira;Amayendayenda mumdima;Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 82