Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 81:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kwanu kusakhale mulungu wafuma kwina;Nusagwadire mulungu wacilendo.

10. Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakukweza kukucotsa ku dziko la Aigupto;Yasamitsa pakamwa pako ndipo ndidzalidzaza.

11. Koma anthu anga sanamvera mau anga;Ndipo Israyeli sanandibvomera.

12. Potero ndinawaperekera kuuma mtima kwao,Ayende monga mwa uphungu wao wao.

13. Ha! akadandimvera anthu anga,Akadayenda m'njira zanga Israyeli!

14. Ndikadagonjetsa adani ao msanga,Ndikadabweza dzanja langa pa owasautsa.

15. Akumuda Yehova akadamgonjera mungakhale monyenga:Koma nyengo yao ikadakhala yosatha,

16. Akadawadyetsa naye tirigu wakometsetsa:Ndikadakukhutitsanso ndi uci wa m'thanthwe.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 81