Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 81:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti ici ndi colemba ca kwa Israyeli,Ciweruzo ca Mulungu wa Yakobo.

5. Anaciika cikhale mboni kwa Yosefe,Pakuturuka iye ku dziko la Aigupto:Komwe ndinamva cinenedwe cosadziwa ine.

6. Ndinamcotsera katundu paphewa pace:Manja ace anamasuka kucotengera.

7. Unaitana posautsika, ndipo ndinakulanditsa;Ndinakubvomereza mobisalika m'bingu;Ndinakuyesa ku madzi a Meriba.

8. Tamvani, anthu anga, ndidzakucitirani mboni;Israyeli, ukadzandimvera!

9. Kwanu kusakhale mulungu wafuma kwina;Nusagwadire mulungu wacilendo.

10. Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakukweza kukucotsa ku dziko la Aigupto;Yasamitsa pakamwa pako ndipo ndidzalidzaza.

11. Koma anthu anga sanamvera mau anga;Ndipo Israyeli sanandibvomera.

12. Potero ndinawaperekera kuuma mtima kwao,Ayende monga mwa uphungu wao wao.

13. Ha! akadandimvera anthu anga,Akadayenda m'njira zanga Israyeli!

Werengani mutu wathunthu Masalmo 81