Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 80:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mutibweze, Mulungu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

4. Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?

5. Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.

6. Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,

7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.

9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.

10. Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.

11. Unatambalitsa mphanda zace mpaka kunyanja,Ndi mitsitsi yace kufikira ku Mtsinje.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 80