Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 80:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mutibweze, Mulungu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

4. Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?

5. Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.

6. Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,

7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.

9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.

10. Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 80