3. Mutibweze, Mulungu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
4. Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?
5. Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.
6. Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,
7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.
9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.
10. Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.