13. Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba,Ndi nyama za kucidikha ziudya,
14. Bwererani, tikupemphani, Mulungu wa makamu;Suzumirani muli m'mwamba, nimupenye, ndi kuzonda mpesa uwu,
15. Ndi tsinde limene dzanja lanu lamanja linaokaeNdi mphanda munadzilimbikitsira.
16. Unapserera ndi moto, unadulidwa;Aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.
17. Dzanja lanu likhale pa munthu wa pa dzanja lamanja lanu;Pa mwana wa munthu amene munadzilimbikitsira.
18. Potero sitidzabwerera m'mbuyo kukusiyani;Titsitsimutseni, ndipo tidzaitanira dzina lanu.
19. Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.