Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 80:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Munapasuliranii maphambo ace,Kotero kuti onse akupita m'njira acherako?

13. Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba,Ndi nyama za kucidikha ziudya,

14. Bwererani, tikupemphani, Mulungu wa makamu;Suzumirani muli m'mwamba, nimupenye, ndi kuzonda mpesa uwu,

15. Ndi tsinde limene dzanja lanu lamanja linaokaeNdi mphanda munadzilimbikitsira.

16. Unapserera ndi moto, unadulidwa;Aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.

17. Dzanja lanu likhale pa munthu wa pa dzanja lamanja lanu;Pa mwana wa munthu amene munadzilimbikitsira.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 80