Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 80:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Unatambalitsa mphanda zace mpaka kunyanja,Ndi mitsitsi yace kufikira ku Mtsinje.

12. Munapasuliranii maphambo ace,Kotero kuti onse akupita m'njira acherako?

13. Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba,Ndi nyama za kucidikha ziudya,

14. Bwererani, tikupemphani, Mulungu wa makamu;Suzumirani muli m'mwamba, nimupenye, ndi kuzonda mpesa uwu,

15. Ndi tsinde limene dzanja lanu lamanja linaokaeNdi mphanda munadzilimbikitsira.

16. Unapserera ndi moto, unadulidwa;Aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.

17. Dzanja lanu likhale pa munthu wa pa dzanja lamanja lanu;Pa mwana wa munthu amene munadzilimbikitsira.

18. Potero sitidzabwerera m'mbuyo kukusiyani;Titsitsimutseni, ndipo tidzaitanira dzina lanu.

19. Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 80