Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 80:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mbusa wa Israyeli, cherani khutu;Inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa;Inu wokhala pa akerubi, walitsani.

2. Utsani camuna canu pamaso pa Efraimu ndi Benjamini ndi Manase,Ndipo mutidzere kutipulumutsa.

3. Mutibweze, Mulungu;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

4. Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?

5. Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.

6. Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,

7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.

9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.

10. Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.

11. Unatambalitsa mphanda zace mpaka kunyanja,Ndi mitsitsi yace kufikira ku Mtsinje.

12. Munapasuliranii maphambo ace,Kotero kuti onse akupita m'njira acherako?

13. Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba,Ndi nyama za kucidikha ziudya,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 80