Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 79:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Anakhetsa mwazi wao ngati madzi pozungulira Yerusalemu;Ndipo panalibe wakuwaika.

4. Takhala cotonza ca anansi athu,Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga,

5. Yehova, mudzakwiya nthawi zonse kufikira liti?Nidzatentha nsanje yanu ngati moto?

6. Thirirani mkwiyo wanu pa akunja osadziwa Inu,Ndi pa maufumu osaitana pa dzina lanu.

7. Pakuti anathera Yakobo,Napasula pokhalira iye.

8. Musakumbukile moritsutsa mphulupulu za makolo athu;Nsoni zokoma zanu zitikumike msanga:Pakuti tafoka kwambiri.

9. Tithandizeni Mulungu wa cipulumutso cathu,Cifukwa ca ulemerero wa dzina lanu;Ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu,Cifukwa ca dzina lanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 79