Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 79:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu, akunja alowa m'colandira canu;Anaipsa Kacisi wanu woyera;Anacititsa Yerusalemu bwinja.

2. Anapereka mitembo ya atumiki anu ikhale cakudya ca mbalame za mlengalenga,Nyama ya okondedwa anu anaipereka kwa zirombo za m'dziko.

3. Anakhetsa mwazi wao ngati madzi pozungulira Yerusalemu;Ndipo panalibe wakuwaika.

4. Takhala cotonza ca anansi athu,Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 79