Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ana a Efraimu okhala nazo zida, oponya nao mauta,Anabwerera m'mbuyo tsiku la nkhondo.

10. Sanasunga cipangano ca Mulungu,Nakana kuyenda m'cilamulo cace.

11. Ndipo anaiwala zocita Iye,Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.

12. Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao,M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.

13. Anagawa nyanja nawapititsapo;Naimitsa madziwo ngati khoma.

14. Ndipo msana anawatsogolera ndi mtamboNdi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.

15. Anang'alula thanthwe m'cipululu,Ndipo anawamwetsa kocuruka monga m'madzi ozama.

16. Anaturukitsa mitsinje m'thanthwe,Inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.

17. Koma anaonjeza kuincimwira Iye,Kupikisana ndi Wam'mwambamwamba m'cipululu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78