Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndi kuti asange makolo ao,Ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu;Mbadwo wosakonza mtima wao,Ndi mzimu wao sunakhazikika ndi Mulungu.

9. Ana a Efraimu okhala nazo zida, oponya nao mauta,Anabwerera m'mbuyo tsiku la nkhondo.

10. Sanasunga cipangano ca Mulungu,Nakana kuyenda m'cilamulo cace.

11. Ndipo anaiwala zocita Iye,Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.

12. Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao,M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78