Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:68-72 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

68. Koma anasankha pfuko la Yuda,Phiri la Ziyoni limene analikonda.

69. Ndipo anamanga malo oyera ace ngati kaphiri,Monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.

70. Ndipo anasankha Davide mtumiki wace,Namtenga ku makola a nkhosa:

71. Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa,Awete Yakobo, anthu ace, ndi Israyeli, colandira cace.

72. Potero anawaweta monga mwa mtima wace wangwiro;Nawatsogolera ndi luso la manja ace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78