Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:55-60 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

55. Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.

56. Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;

57. Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,

58. Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao,Namcititsa nsanje ndi mafano osema.

59. Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;

60. Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo,Cihemaco adacimanga mwa anthu;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78