Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:54-67 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera,Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.

55. Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.

56. Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;

57. Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,

58. Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao,Namcititsa nsanje ndi mafano osema.

59. Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;

60. Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo,Cihemaco adacimanga mwa anthu;

61. Napereka mphamvu yace m'ukapolo,Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.

62. Naperekanso anthu ace kwa lupanga;Nakwiya naco colandira cace.

63. Moto unapsereza anyamata ao;Ndi anamwali ao sanalemekezeka.

64. Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.

65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.

66. Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.

67. Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78