Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:5-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Anakhazika mboni mwa Yakobo,Naika cilamulo mwa Israyeli,Ndizo analamulira atate athu,Akazidziwitse ana ao;

6. Kuti mbadwo ukudzawo udziwe, ndiwo ana amene akadzabadwa;Amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao:

7. Ndi kuti ciyembekezo cao cikhale kwa Mulungu,Osaiwala zocita Mulungu,Koma kusunga malamulo ace ndiko.

8. Ndi kuti asange makolo ao,Ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu;Mbadwo wosakonza mtima wao,Ndi mzimu wao sunakhazikika ndi Mulungu.

9. Ana a Efraimu okhala nazo zida, oponya nao mauta,Anabwerera m'mbuyo tsiku la nkhondo.

10. Sanasunga cipangano ca Mulungu,Nakana kuyenda m'cilamulo cace.

11. Ndipo anaiwala zocita Iye,Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.

12. Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao,M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.

13. Anagawa nyanja nawapititsapo;Naimitsa madziwo ngati khoma.

14. Ndipo msana anawatsogolera ndi mtamboNdi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.

15. Anang'alula thanthwe m'cipululu,Ndipo anawamwetsa kocuruka monga m'madzi ozama.

16. Anaturukitsa mitsinje m'thanthwe,Inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.

17. Koma anaonjeza kuincimwira Iye,Kupikisana ndi Wam'mwambamwamba m'cipululu.

18. Ndipo anayesa Mulungu mumtimamwaoNdi kupempha cakudya monga mwa kulakalaka kwao.

19. Ndipo analankhula motsutsana ndi Mulungu;Anati, Kodi Mulungu akhoza kutikonzera podyera m'cipululu?

20. Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendakoNdi mitsinje inasefuka;Kodi adzakhozanso kupatsa mkate?Kodi adzafunira anthu ace nyama?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78