Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:47-65 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. Anapha mphesa zao ndi matalala,Ndi mikuyu yao ndi cisanu.

48. Naperekanso zoweta zao kwa matalala,Ndi ng'ombe zao kwa mphezi.

49. Anawatumizira mkwiyo wace wotentha,Kuzaza, ndi kupsa mtima, ndi nsautso,Ndizo gulu la amithenga ocita zoipa.

50. Analambulira mkwiyo wace njira;Sanalekerera moyo wao usafe,Koma anapereka moyo wao kumliri;

51. Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Aigupto,Ndiwo oyamba a mphamvu yao m'mahema a Hamu:

52. Koma anaturutsa anthu ace ngati nkhosa,Nawatsogoza ngati gulu la zoweta m'cipululu.

53. Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,Kotero kuti sanaopa;Koma nyanja inamiza adani ao.

54. Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera,Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.

55. Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.

56. Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;

57. Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,

58. Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao,Namcititsa nsanje ndi mafano osema.

59. Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;

60. Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo,Cihemaco adacimanga mwa anthu;

61. Napereka mphamvu yace m'ukapolo,Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.

62. Naperekanso anthu ace kwa lupanga;Nakwiya naco colandira cace.

63. Moto unapsereza anyamata ao;Ndi anamwali ao sanalemekezeka.

64. Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.

65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78