Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:42-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.

43. Amene anaika zizindikilo zace m'Aigupto,Ndi zodabwiza zace ku cidikha ca Zoanu;

44. Nasanduliza nyanja yao mwazi,Ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.

45. Anawatumizira pakati pao mitambo ya nchenche zakuwatha;Ndi acule akuwaononga.

46. Ndipo anapatsa mphuci dzinthu dzao,Ndi dzombe nchito yao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78