Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:39-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.

40. Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.

41. Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.

42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.

43. Amene anaika zizindikilo zace m'Aigupto,Ndi zodabwiza zace ku cidikha ca Zoanu;

44. Nasanduliza nyanja yao mwazi,Ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.

45. Anawatumizira pakati pao mitambo ya nchenche zakuwatha;Ndi acule akuwaononga.

46. Ndipo anapatsa mphuci dzinthu dzao,Ndi dzombe nchito yao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78