Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:37-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Popeza mtima wao sunakonzekera Iye,Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.

38. Koma Iye pokhala ngwa cifundo,Anakhululukira coipa, osawaononga;Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri,Sanautsa ukali wace wonse.

39. Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.

40. Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.

41. Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78