Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:33-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.

34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.

36. Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.

37. Popeza mtima wao sunakonzekera Iye,Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.

38. Koma Iye pokhala ngwa cifundo,Anakhululukira coipa, osawaononga;Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri,Sanautsa ukali wace wonse.

39. Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.

40. Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.

41. Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.

42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.

43. Amene anaika zizindikilo zace m'Aigupto,Ndi zodabwiza zace ku cidikha ca Zoanu;

44. Nasanduliza nyanja yao mwazi,Ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.

45. Anawatumizira pakati pao mitambo ya nchenche zakuwatha;Ndi acule akuwaononga.

46. Ndipo anapatsa mphuci dzinthu dzao,Ndi dzombe nchito yao.

47. Anapha mphesa zao ndi matalala,Ndi mikuyu yao ndi cisanu.

48. Naperekanso zoweta zao kwa matalala,Ndi ng'ombe zao kwa mphezi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78