Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:30-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.

32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.

33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.

34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78