24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.
25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,
26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.
27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:
28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.
29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.
30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,
31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.
32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.
33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.
34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,
35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.
36. Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.