Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:24-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,

26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.

29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.

32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.

33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.

34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78