Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:21-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya;Ndipo anayatsa moto pa Yakobo,Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;

22. Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.

23. Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.

24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,

26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.

29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78