Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira;Ndidzachula zinsinsi zoyambira kale;

3. Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa,Ndipo makolo athu anatifotokozera.

4. Sitidzazibisira ana ao,Koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova,Ndi mphamvu yace, ndi zodabwiza zace zimene anazicita.

5. Anakhazika mboni mwa Yakobo,Naika cilamulo mwa Israyeli,Ndizo analamulira atate athu,Akazidziwitse ana ao;

6. Kuti mbadwo ukudzawo udziwe, ndiwo ana amene akadzabadwa;Amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao:

7. Ndi kuti ciyembekezo cao cikhale kwa Mulungu,Osaiwala zocita Mulungu,Koma kusunga malamulo ace ndiko.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78