Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 78:18-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo anayesa Mulungu mumtimamwaoNdi kupempha cakudya monga mwa kulakalaka kwao.

19. Ndipo analankhula motsutsana ndi Mulungu;Anati, Kodi Mulungu akhoza kutikonzera podyera m'cipululu?

20. Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendakoNdi mitsinje inasefuka;Kodi adzakhozanso kupatsa mkate?Kodi adzafunira anthu ace nyama?

21. Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya;Ndipo anayatsa moto pa Yakobo,Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;

22. Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.

23. Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.

24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,

26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.

29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.

32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.

33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.

34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.

36. Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 78