Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 77:6-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndikumbukila Nyimbo yanga, usiku;Ndilingalira mumtima mwanga;Mzimu wanga unasanthula.

7. Kodi Mulungu adzataya nthawi yonse?Osabwerezanso kukondwera nafe.

8. Cifundo cace calekeka konse konse kodi?Lonjezano lace lidatha kodi ku mibadwo yonse?

9. Kodi Mulungu waiwala kucita cifundo?Watsekereza kodi nsoni zokoma zace mumkwiyo?

10. Ndipo ndinati, Cindilaka ici;Koma ndikumbukila zaka za dzanja lamanja la Wam'mwambamwamba.

11. Ndidzakumbukila zimene adazicita Ambuye;Inde, ndidzakumbukila zodabwiza zanu zoyambira kale.

12. Ndipo ndidzalingalira nchito yanu yonse,Ndi kulingalirabe zimene munazicita Inu.

13. Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu;Mulungu wamkuru ndani monga Mulungu?

14. Inu ndinu Mulungu wakucita codabwiza;Munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15. Munaombola anthu anu ndi mkonowanu,Ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16. Madziwo anakuonani Mulungu;Anakuonani madziwo; anacita mantha:Zozama zomwe zinanjenjemera,

17. Makongwa anatsanula madzi;Thambo lidamvetsa liu lace;Mibvi yanu yomwe inaturukira.

18. Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;Mphezi zinaunikira ponse pali anthu;Dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19. Njira yanu inali m'nyanja,Koyenda Inu nku madzi akulu,Ndipo mapazi anu sanadziwika.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 77