Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 77:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo ndidzalingalira nchito yanu yonse,Ndi kulingalirabe zimene munazicita Inu.

13. Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu;Mulungu wamkuru ndani monga Mulungu?

14. Inu ndinu Mulungu wakucita codabwiza;Munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15. Munaombola anthu anu ndi mkonowanu,Ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16. Madziwo anakuonani Mulungu;Anakuonani madziwo; anacita mantha:Zozama zomwe zinanjenjemera,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 77