Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 77:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzapfuulira kwa Mulungu ndi mau anga;Kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzandicherezera khutu.

2. Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye:Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka;Mtima wanga unakanakutonthozedwa.

3. Ndikumbukila Mulungu ndipo ndibvutika;Ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.

4. Mundikhalitsa maso;Ndigwidwa mtima wosanena kanthu.

5. Ndinaganizira masiku akale, zaka zakalekale.

6. Ndikumbukila Nyimbo yanga, usiku;Ndilingalira mumtima mwanga;Mzimu wanga unasanthula.

7. Kodi Mulungu adzataya nthawi yonse?Osabwerezanso kukondwera nafe.

8. Cifundo cace calekeka konse konse kodi?Lonjezano lace lidatha kodi ku mibadwo yonse?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 77