Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 74:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Otsutsana ndi Inu abangula pakati pa msonkhano wanu;Aika mbendera zao zikhale zizindikilo.

5. Anaoneka ngati osamula nkhwangwa kunkhalango.

6. Ndipo tsopano aphwanya zosemeka zace zonseNdi nkhwangwa ndi nyundo,

7. Anatentha malo anu opatulika;Anaipsa ndi kugwetsa pansi mokhalamo dzina lanu.

8. Ananena mumtima mwao, Tiwapasule pamodzi;Anatentha zosonkhaniramo za Mulungu zonse, m'dzikomo.

9. Sitiziona zizindikilo zathu;Palibenso mneneri;Ndipo mwa ife palibe wina wakudziwa mpaka liti.

10. Wotsutsanayo adzatonza kufikira liti, Mulungu?Kodi mdani adzanyoza dzina lanu nthawi yonse?

11. Mubwezeranji dzanja lanu, ndilo dzanja lamanja lanu?Muliturutse ku cifuwa canu ndipo muwatheretu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 74