21. Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi;Wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.
22. Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha;Kumbukilani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.
23. Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu;Kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakweca kosaleka.