Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 74:12-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma Mulungu ndiye mfumu yanga kuyambira kale,Wocita zakupulumutsa pakati pa dziko lapansi.

13. Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.

14. Mudaphwanya mitu ya livyatanu;Mudampereka akhale cakudya ca iwo a m'cipululu.

15. Mudagawa kasupe ndi mtsinje;Mudaphwetsa mitsinje yaikuru.

16. Usana ndi wanu, usikunso ndi wanu:Munakonza kuunika ndi dzuwa.

17. Munaika malekezero onse a dziko lapansi;Munalenga dzinja ndi malimwe.

18. Mukumbukile ici, Yehova, mdaniyo anatonza,Ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.

19. Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa cirombo;Musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.

20. Samalirani cipanganoco;Pakuti malo amdima a m'dziko adzala ndi zokhalamo ciwawa.

21. Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi;Wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.

22. Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha;Kumbukilani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.

23. Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu;Kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakweca kosaleka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 74