Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 74:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mubwezeranji dzanja lanu, ndilo dzanja lamanja lanu?Muliturutse ku cifuwa canu ndipo muwatheretu.

12. Koma Mulungu ndiye mfumu yanga kuyambira kale,Wocita zakupulumutsa pakati pa dziko lapansi.

13. Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.

14. Mudaphwanya mitu ya livyatanu;Mudampereka akhale cakudya ca iwo a m'cipululu.

15. Mudagawa kasupe ndi mtsinje;Mudaphwetsa mitsinje yaikuru.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 74