Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 73:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Acita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa:Alankhula modzitama.

9. Pakamwa pao anena zam'mwamba,Ndipo lilime lao liyendayenda m'dziko lapansi.

10. Cifukwa cace anthu ace amabwera kudza kuno:Ndipo cikho codzala ndi madzi acigugudiza.

11. Namati, Akacidziwa bwanji Mulungu?Kodi Wam'mwambamwamba ali nayonzeru?

12. Tapenyani, oipa ndi awa;Ndipo pokhazikika cikhazikikire aonjezerapo pa cuma cao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 73