Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 73:21-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;

22. Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu;Ndinali ngati nyama pamaso panu.

23. Koma ndikhala ndi Inu cikhalire:Mwandigwira dzanja langa la manja.

24. Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu,Ndipo mutatero, mudzandilandira m'ulemerero,

25. Ndiri ndi yani Kumwamba, koma Inu?Ndipo Pa dziko lapansi palibe wina wondikonda koma Inu.

26. Likatha thupi langa ndi mtima wanga:Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi colandira canga cosatha.

27. Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka;Muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

28. Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu:Ndimuyesa Ambuye Yehova pathawirapo ine,Kuti ndifotokozere nchito zanu zonse,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 73