Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 73:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pamene ndinayesa kudziwitsa ici,Ndinabvutika naco;

17. Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.

18. Indedi muwaika poterera:Muwagwetsa kuti muwaononge.

19. Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.

20. Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.

21. Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 73