10. Cifukwa cace anthu ace amabwera kudza kuno:Ndipo cikho codzala ndi madzi acigugudiza.
11. Namati, Akacidziwa bwanji Mulungu?Kodi Wam'mwambamwamba ali nayonzeru?
12. Tapenyani, oipa ndi awa;Ndipo pokhazikika cikhazikikire aonjezerapo pa cuma cao.
13. Indedi, ndinayeretsa mtima wanga kwacabe,Ndipo ndinasamba m'manja mosalakwa;
14. Popeza andisautsa tsiku lonse,Nandilanga mamawa monse,
15. Ndikadati, Ndidzafotokozera cotere,Taonani, ndikadacita cosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.
16. Pamene ndinayesa kudziwitsa ici,Ndinabvutika naco;
17. Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.
18. Indedi muwaika poterera:Muwagwetsa kuti muwaononge.
19. Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.
20. Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.
21. Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;
22. Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu;Ndinali ngati nyama pamaso panu.
23. Koma ndikhala ndi Inu cikhalire:Mwandigwira dzanja langa la manja.
24. Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu,Ndipo mutatero, mudzandilandira m'ulemerero,