Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 73:1-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Indedi Mulungu acitira Israyeli zabwino,Iwo a mtima wa mbe.

2. Koma ine, ndikadagwa; Mapazi anga akadaterereka,

3. Pakuti ndinacitira nsanje odzitamandira,Pakuona mtendere wa oipa,

4. Pakuti palibe zomangira pakufa iwo:Ndi mphamvu yao niolimba,

5. Sabvutika monga anthu ena;Sasautsika monga anthu ena.

6. Cifukwa cace kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao;Acibvala ciwawa ngati malaya.

7. Kunenepa kwao kutuzulitsa maso ao:Malingaliro a mitima yao asefukira.

8. Acita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa:Alankhula modzitama.

9. Pakamwa pao anena zam'mwamba,Ndipo lilime lao liyendayenda m'dziko lapansi.

10. Cifukwa cace anthu ace amabwera kudza kuno:Ndipo cikho codzala ndi madzi acigugudiza.

11. Namati, Akacidziwa bwanji Mulungu?Kodi Wam'mwambamwamba ali nayonzeru?

12. Tapenyani, oipa ndi awa;Ndipo pokhazikika cikhazikikire aonjezerapo pa cuma cao.

13. Indedi, ndinayeretsa mtima wanga kwacabe,Ndipo ndinasamba m'manja mosalakwa;

14. Popeza andisautsa tsiku lonse,Nandilanga mamawa monse,

15. Ndikadati, Ndidzafotokozera cotere,Taonani, ndikadacita cosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.

16. Pamene ndinayesa kudziwitsa ici,Ndinabvutika naco;

17. Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 73